20 Kodi uyenera kuyanjana ndi Inu mpando wacifumu wa kusakaza,Wakupanga cobvuta cikhale lamulo?
21 Asonkhana pamodzi pa moyo wa wolungama,Namtsutsa wa mwazi wosacimwa.
22 Koma Yehova wakhala msanje wanga;Ndi Mulungu wanga thanthwe lothawirapo ine.
23 Ndipo anawabwezera zopanda pace zao,Nadzawaononga m'coipa cao;Yehova Mulungu wathu adzawaononga.