10 Aunthama, nawerama,Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.
11 Anena m'mtima mwace, Mulungu waiwala;Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,
12 Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;Musaiwale ozunzika.
13 Woipa anyozeranii Mulungu,Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?
14 Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu;Waumphawi adzipereka kwa Inu;Wamasiye mumakhala mthandizi wace.
15 Thyolani mkono wa woipa;Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.
16 Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;Aonongeka amitundu m'dziko lace.