13 Woipa anyozeranii Mulungu,Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?
14 Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu;Waumphawi adzipereka kwa Inu;Wamasiye mumakhala mthandizi wace.
15 Thyolani mkono wa woipa;Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.
16 Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;Aonongeka amitundu m'dziko lace.
17 Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika:Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:
18 Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.