14 Ameretsa msipu ziudye ng'ombe,Ndi zitsamba acite nazo munthu;Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;
15 Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace,Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.
16 Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi;Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;
17 M'mwemo mbalame zimanga zisa zao;Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,
18 Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma;Pamatanthwe mpothawirapo mbira.
19 Anaika mwezi nyengo zace;Dzuwa lidziwa polowera pace.
20 Muika mdima ndipo pali usiku;Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.