1 Haleluya.Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino:Pakuti cifundo cace ncosatha.
2 Adzafotokoza ndani nchito zamphamvu za Yehova,Adzamveketsa ndani cilemekezo cace conse?
3 Odala iwo amene asunga ciweruzo,Iye amene acita cilungamo nthawi zonse.
4 Mundikumbukile, Yehova, monga momwe mubvomerezana ndi anthu anu;Mundionetsa cipulumutso canu:
5 Kuti ndione cokomaco ca osankhika anu,Kuti ndikondwere naco cikondwerero ca anthu anu,Kuti ndidzitamandire pamodzi ndi colowa canu.