2 Adzafotokoza ndani nchito zamphamvu za Yehova,Adzamveketsa ndani cilemekezo cace conse?
3 Odala iwo amene asunga ciweruzo,Iye amene acita cilungamo nthawi zonse.
4 Mundikumbukile, Yehova, monga momwe mubvomerezana ndi anthu anu;Mundionetsa cipulumutso canu:
5 Kuti ndione cokomaco ca osankhika anu,Kuti ndikondwere naco cikondwerero ca anthu anu,Kuti ndidzitamandire pamodzi ndi colowa canu.
6 Talakwa pamodzi ndi makolo athu;Tacita mphulupulu, tacita coipa.
7 Makolo athu sanadziwitsa zodabwiza zanu m'Aigupto;Sanakumbukila zacifundo zanu zaunyinji;Koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.
8 Koma anawapulumutsa cifukwa ca dzina lace,Kuti adziwitse cimphamvu cace.