158 Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao;Popeza sasamalira mau anu.
159 Penyani kuti ndikonda malangizo anu;Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.
160 Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi;Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.
161 Nduna zinandilondola kopanda cifukwa;Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.
162 Ndikondwera nao mau anu,Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.
163 Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo;Koma ndikonda cilamulo canu.
164 Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi,Cifukwa ca maweruzo anu alungama.