32 Ndidzathamangira njira ya malamulo anu,Mutakulitsa mtima wanga.
33 Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu;Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.
34 Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu;Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.
35 Mundiyendetse mopita malamulo anu;Pakuti ndikondwera m'menemo.
36 Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu,Si ku cisiriro ai.
37 Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe,Mundipatse moyo mu njira yanu.
38 Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.