9 Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;
10 Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.
11 Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:
12 Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.
13 Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.
14 Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza;Nchito zanu nzodabwiza;Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.
15 Thupi langa silinabisikira Inu popangidwa ine mobisika,Poombedwa ine monga m'munsi mwace mwa dziko lapansi.