1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?
2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza;Ndipo usiku, sindikhala cete.
3 Koma Inu ndinu woyera,Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.
4 Makolo athu anakhulupirira Inu:Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.