1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?
2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza;Ndipo usiku, sindikhala cete.
3 Koma Inu ndinu woyera,Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.
4 Makolo athu anakhulupirira Inu:Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.
5 Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa:Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.
6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai:Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.
7 Onse akundipenya andiseka:Akwenzula, apukusa mutu, nati,