5 Munditsogolere m'coonadi canu, ndipo mundiphunzitse;Pakuti Inu ndinu Mulungu wa cipulumutso canga;Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.
6 Kumbukilani, Yehova, nsoni zanu ndi cifundo canu;Pakuti izi nza kale lonse,
7 Musakumbukile zolakwa za ubwana wanga kapena zopikisana nanu:Mundikumbukile monga mwa cifundo canu,Cifukwa ca ubwino wanu, Yehova.
8 Yehova ndiye wabwino ndi wolunjika mtima:Cifukwa cace adzaphunzitsa olawa za njira.
9 Adzawatsogolera ofatsa m'ciweruzo:Ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yace.
10 Mayendedwe onse a Yehova ndiwo cifundo ndi coonadi,Kwa iwo akusunga pangano lace ndi mboni zace.
11 Cifukwa ca dzina lanu, Yehova,Ndikhululukireni kusakaza kwanga, pakuti ndiko kwakukuru.