10 Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo:Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.
11 Ndakhala cotonza cifukwa ca akundisautsa onse,Inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa coopsa:Iwo akundipenya pabwalo anandithawa.
12 Ndaiwalika m'mtima monga wakufa:Ndikhala monga cotengera cosweka.
13 Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,Mantha andizinga:Pondipangira ciwembu,Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.
14 Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,
15 Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu:Mundipulumutse ndi cifundo canu.