4 Mundionjole m'ukonde umene anandichera mobisika.Pakuti Inu ndinu mphamvu yanga.
5 Ndipereka mzimu wanga m'dzanja lanu:Mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa coonadi.
6 Ndikwiya nao iwo akusamala zacabe zonama:Koma ndikhulupirira Yehova.
7 Ndidzakondwera ndi kusangalala m'cifundo canu:Pakuti mudapenya zunzo langa;Ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga:
8 Ndipo simunandipereka m'dzanja la mdani;Munapondetsa mapazi anga pali malo.
9 Mundicitire cifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine:Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga, zapuwala ndi mabvuto,
10 Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo:Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.