8 Ndipo simunandipereka m'dzanja la mdani;Munapondetsa mapazi anga pali malo.
9 Mundicitire cifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine:Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga, zapuwala ndi mabvuto,
10 Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo:Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.
11 Ndakhala cotonza cifukwa ca akundisautsa onse,Inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa coopsa:Iwo akundipenya pabwalo anandithawa.
12 Ndaiwalika m'mtima monga wakufa:Ndikhala monga cotengera cosweka.
13 Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,Mantha andizinga:Pondipangira ciwembu,Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.
14 Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova:Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,