9 Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako,Kapena mbuzi m'makola mwako.
10 Pakuti zamoyo zonse za kuthengo ndi zanga,Ndi ng'ombe za pa mapiri zikwi.
11 Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri:Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.
12 Ndikamva njala, sindidzakuuza:Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.
13 Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe,Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?
14 Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko;Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:
15 Ndipo undiitane tsiku la cisautso:Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.