13 Koma ine, pemphero langa liri kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika;Mulungu, mwa cifundo canu cacikuru,Mundibvomereze ndi coonadi ca cipulumutso canu.
14 Mundilanditse kuthope, ndisamiremo:Ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama.
15 Cigumula cisandifotsere,Ndipo cakuya cisandimize;Ndipo asanditsekere pakamwa pace pa dzenje.
16 Mundiyankhe Yehova; pakuti cifundo canu ncokoma;Munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu.
17 Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu;Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.
18 Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola;Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,
19 Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga:Akundisautsa ali pamaso panu,