8 Abale anga andiyesa mlendo,Ndi ana a mai wanga andiyesa wa mtundu wina.
9 Pakuti cangu ca pa nyumba yanu candidya;Ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.
10 Ndipo ndinalira pa kusala kwa moyo wanga,Koma uku kunandikhalira cotonza.
11 Ndipo cobvala canga ndinayesa ciguduli,Koma amandiphera mwambi.
12 Okhala pacipata akamba za ine; Ndipo oledzera andiyimba.
13 Koma ine, pemphero langa liri kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika;Mulungu, mwa cifundo canu cacikuru,Mundibvomereze ndi coonadi ca cipulumutso canu.
14 Mundilanditse kuthope, ndisamiremo:Ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama.