36 Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.
37 Popeza mtima wao sunakonzekera Iye,Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.
38 Koma Iye pokhala ngwa cifundo,Anakhululukira coipa, osawaononga;Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri,Sanautsa ukali wace wonse.
39 Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.
40 Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.
41 Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.
42 Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.