1 Yehova acita ufumu; dziko lapansi likondwere;Zisumbu zambiri zikondwerere.
2 Pomzinga pali mitambo ndi mdima;Cilungamo ndi ciweruzo ndizo zolimbitsa mpando wacifumu wace.
3 Moto umtsogolera,Nupsereza otsutsana naye pozungulirapo,
4 Mphezi zace zinaunikira dziko lokhalamo anthu;Dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.