3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;Muyimbire zolemekeza dzina lace; pakuti nkokondweretsa kutero.
4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,Israyeli, akhale cuma cace ceni ceni.
5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkuru,Ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.
6 Ciri conse cimkonda Yehova acicita,Kumwamba ndi pa dziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.
7 Akweza mitambo icokere ku malekezero a dziko lapansi;Ang'animitsa mphezi zidzetse mvula;Aturutsa mphepo mosungira mwace.
8 Anapanda oyamba a Aigupto,Kuyambira munthu kufikira zoweta.
9 Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako,Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.