12 Kuti ana athu amuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime;Ana athu akazi ngati nsanamira za kungondya, zosema zikometsere nyumba ya mfumu.
13 Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundu mitundu;Ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwi zikwi, inde zikwi khumi kubusako.
14 Kuti ng'ombe zathu zikhale zasenza katundu;Ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kuturukamo,Pasakhalenso kupfuula m'makwalala athu.
15 Odala anthu akuona zotere; Odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.