20 Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa ciwembu ca munthu:Mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.
21 Wolemekezeka Yehova:Pakuti anandicitira cifundo cace codabwiza m'mudzi walinga.
22 Ndipo ine, pakutenga nkhawa, ndinati, Ndadulidwa kundicotsa pamaso panu:Komatu munamva mau a kupemba kwanga pamene ndinapfuulira kwa Inu.
23 Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ace:Yehova asunga okhulupirika,Ndipo abwezera zocuruka iye wakucita zodzitama.
24 Limbikani, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu,Inu nonse akuyembekeza Yehova.