3 Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete:Moto udzanyeka pankhope pace,Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.
4 Kumwamba adzaitana zakumwamba,Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:
5 Mundisonkhanitsire okondedwa anga;Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.
6 Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace;Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.
7 Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena;Israyeli, ndipo ndidzacita mboni pa iwe:Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.
8 Sindikudzudzula iwe cifukwa ca nsembe zako;Popeza nsembe zako zopsereza ziri pamaso panga cikhalire.
9 Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako,Kapena mbuzi m'makola mwako.